1 Akorinto 10:2-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. nabatizidwa onse kwa Mose, mumtambo, ndi m'nyanja,

3. nadya onse cakudya cauzimu cimodzimodzi;

4. namwa onse cakumwa cauzimu cimodzimodzi; pakuti anamwa mwa thanthwe lauzimu lakuwatsata; koma thanthwelo ndiye Kristu.

5. Koma ocuruka a iwo Mulungu sanakondwera nao; pakuti anamwazika m'cipululu.

6. Koma zinthu izi zinacitika, zikhale zoticenjeza ife, kuti tisalakalake zoipa ife, monganso iwowo analakalaka.

7. Kapena musakhale opembedza mafano, monga ena a iwo, monga kwalembedwa, Anthu anakhala pansi kudya ndi kumwa, nanyamuka kusewera.

8. Kapena tisacite dama monga ena a iwo anacita dama, nagwa tsiku limodzi zikwi makumi awiri ndi zitatu.

1 Akorinto 10