19. Ndinena ciani tsono? kuti coperekedwa nsembe kwa mafano ciri kanthu? Kapena kuti fane liri kanthu kodi?
20. Koma nditi kuti zimene amitundu apereka nsembe azipereka kwa ziwanda; ndipo sindifuna kuti inu muyanjane ndi ziwanda.
21. Simungathe kumwera cikho ca Ambuye, ndi cikho ca ziwanda; simungathe kulandirako ku gome la Ambuye, ndi ku gome la ziwanda.
22. Kapena kodi ticititsa nsanje Ambuye? Kodi mphamvu zathu ziposa iye?